1
AROMA 15:13
Buku Lopatulika
BLP-2018
Ndipo Mulungu wa chiyembekezo adzaze inu ndi chimwemwe chonse ndi mtendere m'kukhulupirira, kuti mukachuluke ndi chiyembekezo, mu mphamvu ya Mzimu Woyera.
Compare
Explore AROMA 15:13
2
AROMA 15:4
Pakuti zonse zinalembedwa kale zinalembedwa kutilangiza, kuti mwa chipiriro ndi chitonthozo cha malembo, tikhale ndi chiyembekezo.
Explore AROMA 15:4
3
AROMA 15:5-6
Ndipo Mulungu wa chipiriro ndi wa chitonthozo apatse inu kuti mukhale ndi mtima umodzi wina ndi mnzake, monga mwa Khristu Yesu; kuti nonse pamodzi, m'kamwa mmodzi, mukalemekeze Mulungu ndi Atate wa Ambuye wathu Yesu Khristu.
Explore AROMA 15:5-6
4
AROMA 15:7
Chifukwa chake mulandirane wina ndi mnzake, monganso Khristu anakulandirani inu, kukachitira Mulungu ulemerero.
Explore AROMA 15:7
5
AROMA 15:2
Yense wa ife akondweretse mnzake, kumchitira zabwino, zakumlimbikitsa.
Explore AROMA 15:2