1
MATEYU 15:18-19
Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014
BLPB2014
Koma zakutuluka m'kamwa zichokera mumtima; ndizo ziipitsa munthu. Pakuti mumtima muchokera maganizo oipa, zakupha, zachigololo, zachiwerewere, zakuba, za umboni wonama, zamwano
Linganisha
Chunguza MATEYU 15:18-19
2
MATEYU 15:11
si chimene chilowa m'kamwa mwake chiipitsa munthu; koma chimene chituluka m'kamwa mwake, ndicho chiipitsa munthu.
Chunguza MATEYU 15:11
3
MATEYU 15:8-9
Anthu awa andilemekeza Ine ndi milomo yao; koma mtima wao uli kutali ndi Ine. Koma andilambira Ine kwachabe, ndi kuphunzitsa maphunzitso, malangizo a anthu.
Chunguza MATEYU 15:8-9
4
MATEYU 15:28
Pomwepo Yesu anayankha, nati kwa iye, Mkaziwe, chikhulupiriro chako ndi chachikulu; chikhale kwa iwe monga momwe wafunira. Ndipo mwana wake anachira nthawi yomweyo.
Chunguza MATEYU 15:28
5
MATEYU 15:25-27
Koma iye anadza, namgwadira Iye, nanena, Ambuye, ndithangateni ine. Ndipo Iye anayankha, nati, Sichabwino kutenga mkate wa ana, ndi kuuponyera tiagalu. Koma iye anati, Etu, Ambuye, pakutinso tiagalu timadya nyenyeswa zakugwa pagome pa ambuye ao.
Chunguza MATEYU 15:25-27
Nyumbani
Biblia
Mipango
Video