1
1 AKORINTO 2:9
Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014
BLPB2014
koma monga kulembedwa, Zimene diso silinaziona, ndi khutu silinazimva, nisizinalowa mu mtima wa munthu, zimene zilizonse Mulungu anakonzereratu iwo akumkonda Iye.
Linganisha
Chunguza 1 AKORINTO 2:9
2
1 AKORINTO 2:14
Koma munthu wa chibadwidwe cha umunthu salandira za Mzimu wa Mulungu: pakuti aziyesa zopusa; ndipo sakhoza kuzizindikira, chifukwa ziyesedwa mwauzimu.
Chunguza 1 AKORINTO 2:14
3
1 AKORINTO 2:10
Koma kwa ife Mulungu anationetsera izi mwa Mzimu; pakuti Mzimu asanthula zonse, zakuya za Mulungu zomwe.
Chunguza 1 AKORINTO 2:10
4
1 AKORINTO 2:12
Koma sitinalandira ife mzimu wa dziko lapansi, koma Mzimu wa kwa Mulungu, kuti tikadziwe zimene zipatsidwa kwa ife ndi Mulungu kwaufulu.
Chunguza 1 AKORINTO 2:12
5
1 AKORINTO 2:4-5
Ndipo mau anga ndi kulalikira kwanga sanakhala ndi mau okopa a nzeru, koma m'chionetso cha Mzimu ndi cha mphamvu; kuti chikhulupiriro chanu chisakhale m'nzeru ya anthu, koma mu mphamvu ya Mulungu.
Chunguza 1 AKORINTO 2:4-5
Nyumbani
Biblia
Mipango
Video