1
MATEYU 12:36-37
Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014
BLPB2014
Ndipo ndinena kwa inu, kuti mau onse opanda pake, amene anthu adzalankhula, adzawawerengera mlandu wake tsiku la kuweruza. Pakuti udzayesedwa wolungama ndi mau ako, ndipo ndi mau ako omwe udzatsutsidwa.
Linganisha
Chunguza MATEYU 12:36-37
2
MATEYU 12:34
Akubadwa inu a njoka, mungathe bwanji kulankhula zabwino, inu akukhala oipa? Pakuti m'kamwa mungolankhula mwa kusefuka kwake kwa mtima.
Chunguza MATEYU 12:34
3
MATEYU 12:35
Munthu wabwino atulutsa zabwino m'chuma chake chabwino, ndi munthu woipa atulutsa zoipa m'chuma chake choipa.
Chunguza MATEYU 12:35
4
MATEYU 12:31
Chifukwa chake ndinena kwa inu, Machimo onse, ndi zonena zonse zamwano, zidzakhululukidwa kwa anthu; koma chamwano cha pa Mzimu Woyera sichidzakhululukidwa.
Chunguza MATEYU 12:31
5
MATEYU 12:33
Ukakoma mtengo, chipatso chake chomwe chikoma; ukaipa mtengo, chipatso chake mtengo udziwika.
Chunguza MATEYU 12:33
Nyumbani
Biblia
Mipango
Video