1
Marko 14:36
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
CCL
Iye anati, “Abba, Atate, zinthu zonse ndi zotheka ndi Inu. Chotsereni chikhochi. Komabe chitani zimene Inu mukufuna, osati zimene Ine ndikufuna.”
Yenzanisa
Ongorora {{vhesi}}
2
Marko 14:38
Khalani tcheru ndi kupemphera kuti musalowe mʼmayesero. Mzimu ukufuna, koma thupi ndi lofowoka.”
3
Marko 14:9
Zoonadi, ndikuwuzani kuti kulikonse kumene Uthenga Wabwino udzalalikidwa pa dziko lonse, zimene wachitazi zidzanenedwa pomukumbukira iye.”
4
Marko 14:34
Iye anawawuza kuti, “Moyo wanga wagwidwa ndi chisoni chofa nacho. Khalani pano ndipo musagone.”
5
Marko 14:22
Pamene ankadya, Yesu anatenga buledi, nayamika ndipo anamunyema nagawira ophunzira ake nanena kuti, “Tengani, ili ndi thupi langa.”
6
Marko 14:23-24
Kenaka anatenga chikho, nayamika nachipereka kwa iwo ndipo onse anamweramo. Iye anawawuza kuti, “Awa ndi magazi anga a pangano amene akhetsedwa chifukwa cha ambiri.
7
Marko 14:27
Yesu anati, “Nonse mudzandithawa, pakuti kwalembedwa: “ ‘Kantha Mʼbusa, ndipo nkhosa zidzabalalika.’
8
Marko 14:42
Nyamukani! Tiyeni tizipita! Uyu wondipereka Ine wafika!”
9
Marko 14:30
Yesu anayankha kuti, “Zoona ndikukuwuza kuti lero lino, usiku uno, tambala asanalire kawiri, iweyo udzandikana katatu.”