1
Yoh. 10:10
Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa
BLY-DC
Wakuba amangodzera kuba, kupha ndi kuwononga. Koma Ine ndidabwera kuti nkhosazo zikhale ndi moyo, moyo wake wochuluka.
Comparer
Explorer Yoh. 10:10
2
Yoh. 10:11
“Ine ndine mbusa wabwino. Mbusa wabwino amataya moyo wake chifukwa cha nkhosa zake.
Explorer Yoh. 10:11
3
Yoh. 10:27
Nkhosa zanga zimamva mau anga. Ine ndimazidziŵa, ndipo zimanditsatira.
Explorer Yoh. 10:27
4
Yoh. 10:28
Ndimazipatsa moyo wosatha, ndipo sizidzatayika konse. Palibe munthu wodzazilanda m'manja mwanga.
Explorer Yoh. 10:28
5
Yoh. 10:9
Khomo ndine. Munthu akaloŵera pa Ine, adzapulumuka. Azidzaloŵa ndi kutuluka, ndipo adzapeza chakudya.
Explorer Yoh. 10:9
6
Yoh. 10:14
Mbusa wabwino ndine. Nkhosa zanga ndimazidziŵa, ndipo izozo Ineyo zimandidziŵa
Explorer Yoh. 10:14
7
Yoh. 10:29-30
Atate anga amene adandipatsa nkhosazo amapambana onse, ndipo palibe amene angathe kuzilanda m'manja mwao. Ine ndi Atate ndife amodzi.”
Explorer Yoh. 10:29-30
8
Yoh. 10:15
monga momwe Atate amadziŵira Ine, nanenso nkuŵadziŵa Atatewo. Ndimatayirapo moyo wanga pa nkhosazo.
Explorer Yoh. 10:15
9
Yoh. 10:18
Palibe munthu wondilanda moyo wangawu, koma ndikuupereka ndekha. Ndili nazo mphamvu zoutaya moyo wanga, ndili nazonso mphamvu zoutenganso. Udindo umenewu ndidaulandira kwa Atate anga.”
Explorer Yoh. 10:18
10
Yoh. 10:7
Tsono Yesu adatinso, “Ndithu ndikunenetsa kuti Ine ndine khomo la nkhosa.
Explorer Yoh. 10:7
11
Yoh. 10:12
Koma wolembedwa ntchito chabe akaona mmbulu ulikudza, amazisiya nkhosazo iye nkuthaŵa. Amatero popeza kuti si mbusa weniweni, ndipo nkhosa si zake ai. Tsono mmbulu uja umagwirapo zina, zina nkumwazikana.
Explorer Yoh. 10:12
12
Yoh. 10:1
“Kunena zoona, munthu woloŵa m'khola la nkhosa osadzera pa khomo, koma kuchita kukwerera pena, ameneyo ndi wakuba ndi wolanda.
Explorer Yoh. 10:1
Accueil
Bible
Plans
Vidéos