Matayo 8
8
Yesu wamlamicha mundhu wa makate
Maluko 1:40-45; Luka 5:12-16
1Yesu yapo wadachika kuphili, gulu la likulu la wandhu lidamchata. 2Mundhu mmojhi uyo wadali ni makate wadamchata Yesu, wadamgwadila ni kukamba, “Ambuye, mkafuna, mkoza kunilamicha kuti nikhoze kumlambila Mnungu!”
3Yesu wadatambasula jhanja lake, nikumgafya wodwalayo ni kumkambila, “Nifuna! Ulame.” Pampajha mundhuyo wadalama makate yake. 4Ndiipo Yesu wadamkambila, “Vechela, usadamkambila mundhu waliyonjhe, nambho pita ukajhilangize kwa ajhukulu, ni kuchocha njhembe iyo yalamulidwa ni Musa kuwachimikhizila wandhu wonjhe kuti walama.”
Yesu wamlamicha mbowa wa mkulu wa loma
Luka 7:1-10
5Yesu yapo wadalowa ku Kapelinaumu, wamkulu wa gulu la asilikali mmojhi wa kuloma, wadamchata ni wadampembha wamthangatile. 6Ndiipo wadakamba, “Imwe Ambuye, mbowa wanga wagona kukhomo, wavuwala ni wadwala kupunda.”
7Yesu wadamkambila, “Sinijhe kumlamicha.”
8Nambho yujha wamkulu waloma wadamkambila, “Imwe Ambuye, ine sinifunika imwe mulowe mnyumba mwanga, nambho chochani lamulope, ni mbowa wanga siwalame. 9Pakuti ata ine nichogozedwa ni waakuluakulu wina, nilinawo asikali yao naachogoza. Nimlamula mmojhi, ‘Pita!’ Nayo wapita, ‘Majha!’ Nayo wakujha ni mbowa wanga, ‘Chita chindhu ichi! Nayo wachita.’ ”
10Yesu yapo wadavela chimwecho, wadazizwa, wadaakambila wandhu wajha adamchata, “Zene nikukambilani, sinidaone mundhu waliyonjhe mujhiko la Izilaeli uyo wali ni chikhulupi ngati ichi. 11Zenedi nikukambilani, wandhu ambili siajhe kuchokela dela la kumwela ni kumpoto, nawo siakhale papwando pamojhi ni Ibulahimu ni Isaka ni Yakobo pa ufumu wa kumwamba. 12Nambho wajha amafunika kukhala mu ufumu wa Mnungu saataidwe kubwalo mumdima, uko sikukhale chililo ni kukukuta mano.” 13Ndiipo Yesu wadamkambila yujha wamkulu wa Loma, “Pita kukhomo, ni ikhale ngati umo wakhulupilila.”
Ni mbowa wake wadalama saa imweijha.
Yesu waalamicha wandhu ambili
Maluko 1:29-34; Luka 4:38-41
14Yesu wadafika kukhomo kwa Petulo, wadakomana apongozi wakazi Apetulo agona pachithanda, adwala matenda. 15Yesu wadagafya jhanja la maye mmeneyo, ndhenda idamchoka, nayo wadanyakuka ni kuyamba kumuandalia chakudya.
16Ujhulo yapo udafika, wandhu adampelekela Yesu wandhu ambili yawo adazamwa ni viwanda, Yesu wadavitopola viwanda, ni kwaalamicha odwala onjhe. 17Wadachita chimwecho kuti yakwanile malembo ya mlosi Isaya, “Iye mwenewake watenga mavuto yathu, ni watenga matenda yathu.”
Ochatila a Yesu umo afunika kukhala
Luka 9:57-62
18Yesu yapo wadaliona gulu lalikulu la wandhu lamzungulila, wadalamula oyaluzidwa wake apite kuchijya la nyanja ya Galilaya. 19Oyaluza thauko wadamsendelela, wadamkambila, “Oyaluza, sinikuchateni kwalikonjhe uko simpite.”
20Yesu wadayangha, “Nghandwe zali ni mbhanga, ni mbalami zali nivisa nambho mwana wa mundu walibe malo yo gona.”
21Mmojhi wa oyaluzidwa wake wadamkambila, “Ambuye, mniloleze uti nikaazike atate wanga.”
22Yesu wadamuyangha, “Nichate! Aleke wandhu yawo ali ngati amwalila azike wandhu yawo amwalila.”
Yesu watuliza mwela
Maluko 4:35-41; Luka 8:22-25
23Yesu wadakwela mboti, ni oyaluzidwa wake adamchata. 24Pampajha kudachokela mwela mnyanja, ata mafunde yadayamba kulibula boti. Yesu wadando gona litulo. 25Oyaluzidwa adamchata, adamuucha nikukamba, “Ambuye, tilamicheni, titobila!”
26Yesu wadaayangha, “Imwe wandhu achikulupi chochepa, ndandeyanji muopa?” Yesu wadaima nukutuliza mwela ni nyanja idagona.
27Wandhu adadabwa, adajhifunjha, “Mundhu wabwanji uyu? Ata mbhepo ni mafunde vimvela!”
Yesu walamicha wandhu awili a viwanda
Maluko 5:1-20; Luka 8:26-39
28Yesu yapo wadafika kuchijha la nyanja mujhiko la Agadala, wadakomana ni wandhu awili yao amachoka kumainja, azamwa ni chiwanda. Wandhuwo adali owofya kupunda ni padalibe mundhu uyo wamapita mnjila imeneyo. 29Pampajha adayamba kubula mapokoso, “Ufuna chiyani kwaife, iwe Mwana wa Mnungu? Bwanji, wajha kutivuticha ndhawi ikali yosakwanila?”
30Pafupi ni malo yameyo padali nguluwe zambili zidali kudyela. 31Ndiipo viwanda vidampembha Yesu, “Ngati utichocha tuloleze tikazilowe nguluwe zijha.”
32Yesu wadavikambila, “Haya pitani.” Pamwepo lijha gulu la viwanda lidaachoka wandhu, lidalowa kwa nguluwe, ni gulu lonjhe la nguluwe lidachika pamchikililo nikufela mmajhi.
33Wandhu owesa nguluwe wajha adathawa, adapita kumujhi. Kumeneko adakambilila nghani zijha zidaachokela wajha adazamwa ni viwanda. 34Ndiipo, wandhu wonjhe adapita kukomana ni Yesu, adampembha kupunda wachoke mujhiko lao.
Actualmente seleccionado:
Matayo 8: NTNYBL2025
Destacar
Compartir
Copiar

¿Quieres tener guardados todos tus destacados en todos tus dispositivos? Regístrate o inicia sesión
The New Testament in Nyanja @The Word for The World International and Nyanja Language translation, 2025. All rights reserved.
Matayo 8
8
Yesu wamlamicha mundhu wa makate
Maluko 1:40-45; Luka 5:12-16
1Yesu yapo wadachika kuphili, gulu la likulu la wandhu lidamchata. 2Mundhu mmojhi uyo wadali ni makate wadamchata Yesu, wadamgwadila ni kukamba, “Ambuye, mkafuna, mkoza kunilamicha kuti nikhoze kumlambila Mnungu!”
3Yesu wadatambasula jhanja lake, nikumgafya wodwalayo ni kumkambila, “Nifuna! Ulame.” Pampajha mundhuyo wadalama makate yake. 4Ndiipo Yesu wadamkambila, “Vechela, usadamkambila mundhu waliyonjhe, nambho pita ukajhilangize kwa ajhukulu, ni kuchocha njhembe iyo yalamulidwa ni Musa kuwachimikhizila wandhu wonjhe kuti walama.”
Yesu wamlamicha mbowa wa mkulu wa loma
Luka 7:1-10
5Yesu yapo wadalowa ku Kapelinaumu, wamkulu wa gulu la asilikali mmojhi wa kuloma, wadamchata ni wadampembha wamthangatile. 6Ndiipo wadakamba, “Imwe Ambuye, mbowa wanga wagona kukhomo, wavuwala ni wadwala kupunda.”
7Yesu wadamkambila, “Sinijhe kumlamicha.”
8Nambho yujha wamkulu waloma wadamkambila, “Imwe Ambuye, ine sinifunika imwe mulowe mnyumba mwanga, nambho chochani lamulope, ni mbowa wanga siwalame. 9Pakuti ata ine nichogozedwa ni waakuluakulu wina, nilinawo asikali yao naachogoza. Nimlamula mmojhi, ‘Pita!’ Nayo wapita, ‘Majha!’ Nayo wakujha ni mbowa wanga, ‘Chita chindhu ichi! Nayo wachita.’ ”
10Yesu yapo wadavela chimwecho, wadazizwa, wadaakambila wandhu wajha adamchata, “Zene nikukambilani, sinidaone mundhu waliyonjhe mujhiko la Izilaeli uyo wali ni chikhulupi ngati ichi. 11Zenedi nikukambilani, wandhu ambili siajhe kuchokela dela la kumwela ni kumpoto, nawo siakhale papwando pamojhi ni Ibulahimu ni Isaka ni Yakobo pa ufumu wa kumwamba. 12Nambho wajha amafunika kukhala mu ufumu wa Mnungu saataidwe kubwalo mumdima, uko sikukhale chililo ni kukukuta mano.” 13Ndiipo Yesu wadamkambila yujha wamkulu wa Loma, “Pita kukhomo, ni ikhale ngati umo wakhulupilila.”
Ni mbowa wake wadalama saa imweijha.
Yesu waalamicha wandhu ambili
Maluko 1:29-34; Luka 4:38-41
14Yesu wadafika kukhomo kwa Petulo, wadakomana apongozi wakazi Apetulo agona pachithanda, adwala matenda. 15Yesu wadagafya jhanja la maye mmeneyo, ndhenda idamchoka, nayo wadanyakuka ni kuyamba kumuandalia chakudya.
16Ujhulo yapo udafika, wandhu adampelekela Yesu wandhu ambili yawo adazamwa ni viwanda, Yesu wadavitopola viwanda, ni kwaalamicha odwala onjhe. 17Wadachita chimwecho kuti yakwanile malembo ya mlosi Isaya, “Iye mwenewake watenga mavuto yathu, ni watenga matenda yathu.”
Ochatila a Yesu umo afunika kukhala
Luka 9:57-62
18Yesu yapo wadaliona gulu lalikulu la wandhu lamzungulila, wadalamula oyaluzidwa wake apite kuchijya la nyanja ya Galilaya. 19Oyaluza thauko wadamsendelela, wadamkambila, “Oyaluza, sinikuchateni kwalikonjhe uko simpite.”
20Yesu wadayangha, “Nghandwe zali ni mbhanga, ni mbalami zali nivisa nambho mwana wa mundu walibe malo yo gona.”
21Mmojhi wa oyaluzidwa wake wadamkambila, “Ambuye, mniloleze uti nikaazike atate wanga.”
22Yesu wadamuyangha, “Nichate! Aleke wandhu yawo ali ngati amwalila azike wandhu yawo amwalila.”
Yesu watuliza mwela
Maluko 4:35-41; Luka 8:22-25
23Yesu wadakwela mboti, ni oyaluzidwa wake adamchata. 24Pampajha kudachokela mwela mnyanja, ata mafunde yadayamba kulibula boti. Yesu wadando gona litulo. 25Oyaluzidwa adamchata, adamuucha nikukamba, “Ambuye, tilamicheni, titobila!”
26Yesu wadaayangha, “Imwe wandhu achikulupi chochepa, ndandeyanji muopa?” Yesu wadaima nukutuliza mwela ni nyanja idagona.
27Wandhu adadabwa, adajhifunjha, “Mundhu wabwanji uyu? Ata mbhepo ni mafunde vimvela!”
Yesu walamicha wandhu awili a viwanda
Maluko 5:1-20; Luka 8:26-39
28Yesu yapo wadafika kuchijha la nyanja mujhiko la Agadala, wadakomana ni wandhu awili yao amachoka kumainja, azamwa ni chiwanda. Wandhuwo adali owofya kupunda ni padalibe mundhu uyo wamapita mnjila imeneyo. 29Pampajha adayamba kubula mapokoso, “Ufuna chiyani kwaife, iwe Mwana wa Mnungu? Bwanji, wajha kutivuticha ndhawi ikali yosakwanila?”
30Pafupi ni malo yameyo padali nguluwe zambili zidali kudyela. 31Ndiipo viwanda vidampembha Yesu, “Ngati utichocha tuloleze tikazilowe nguluwe zijha.”
32Yesu wadavikambila, “Haya pitani.” Pamwepo lijha gulu la viwanda lidaachoka wandhu, lidalowa kwa nguluwe, ni gulu lonjhe la nguluwe lidachika pamchikililo nikufela mmajhi.
33Wandhu owesa nguluwe wajha adathawa, adapita kumujhi. Kumeneko adakambilila nghani zijha zidaachokela wajha adazamwa ni viwanda. 34Ndiipo, wandhu wonjhe adapita kukomana ni Yesu, adampembha kupunda wachoke mujhiko lao.
Actualmente seleccionado:
:
Destacar
Compartir
Copiar

¿Quieres tener guardados todos tus destacados en todos tus dispositivos? Regístrate o inicia sesión
The New Testament in Nyanja @The Word for The World International and Nyanja Language translation, 2025. All rights reserved.