Matayo 14
14
Kumwalila kwa Yohana Mbatizi
Maluko 6:14-29; Luka 9:7-9
1Ndhawi imeneyo Helode, mfumu wa Galilaya wadavela nghani za Yesu. 2Ndiipo wadaakambila, mbowa wake, “Mundhu uyu ni Yohana Mbatizi, wahyuka. Ndendande wali ni mbhavu zochita vozizwicha.”
3Helode ndeuyo wadamgwila Yohana ni kumuika mndende ndande ya Helodia, mkazi wa Filipo mpwake. 4Ndande Yohana wadamkambila Helode tetete, “Osati bwino iwe kumkwata wamkazi mmeneyo!” 5Helode wamafuna kumpha Yohana, nambho wadaopa wandhu ndande wandhu adakhulupilila kuti Yohana ni mlosi.
6Siku la pwando la kubadwa kwa Helode, mwali wa Helodia wadavina pachogolo pa alendo, Helode wadakondwela kupunda, 7mbaka wadamkambila kuti, “Sinikupache chalichonjhe icho siunipembhe.”
8Ndiipo, amake adamuyaluza chopita kupembha, mwaliyo wadakamba, “Nipache mutu wa Yohana Mbatizi mliselo.”
9Mfumu wadavela chisoni, nambho ndande ya kulumbila kwake pachogolo pa alendo wake, wadalamula mwaliyo wapachidwe icho wadapembha. 10Chimwecho, Helode wadamtuma asikali wamdule mutu Yohana kujha kundende. 11Mutu wa Yohana udaikidwa mliselo ni kupachidwa mwali yujha, nayo wadaapelekela maye wake. 12Oyaluzidwa a Yohana adajha, adatenga chitanda cha Yohana, adachizika. Ndiipo adapita kumkambila Yesu nghani zimenezo.
Yesu waaningha chakudya wandhu kupitilila elfu zisano
Maluko 6:30-44; Luka 9:10-17; Yohana 6:1-14
13Yesu yapo wadavela nghani za Yohana, wadachoka malo yajha kwa boti, wadapita pamalo popande wandhu kuti wakhale yokha. Nambho wandhu yapo adavela adamchata poyenda pa mwendo kuchokela mmijhi yao. 14Yesu yapo wadachika mboti, wadaliona gulu lalikulu la wandhu, wadaonela lisungu ni wadaalamicha odwala wao.
15Ujhulo yapo udafika, oyaluzidwa wake adamchata ni kumkambila, “Malo yano ni paphululu, jhuwa litobila. Walole wandhu apite kumijhi akajhigulile chakudya.”
16Yesu wadaakambila, “Siifunika achoke, anyiimwe mwachinawene wake mwaapache chakudya.”
17Anyiiwo adamuyangha, “Tulinayo mabumunda isanope ni njhomba ziwili.”
18Yesu wadaakambila, “Nipelekeleni pano.” 19Wadaakambila wandhu akhale mmaujhu. Yesu wadatenga mabumunda yasano ni njhombha ziwili zijha, wadakweza maso yake kumwamba, wadamyamika Mnungu. Halafu wadabandhula mabumunda ni kwaapacha oyaluzidwa wake, naonjho oyaluzidwa wake wadaagawila wandhu. 20Wandhu wonjhe adadya ni kukhuta. Oyaluzidwa adakokola vidufya ivo vidakhalila ni kujhaza miseche khumi ni iwili. 21Wachimuna yawo adadya adali ngati elufu zisano, nambho waachikazi ni wana siadawelengedwe.
Yesu wayenda pa mwamba pa majhi
Maluko 6:45-52; Yohana 6:15-21
22Yesu yapo wamalaila wandhu, wadaakambila oyaluzidwa wake akwele mbwato wa ukulu kuti achogolele kupita kuchijya kwa nyanja ya Galilaya. 23Yapo wadamaliza kwalaila wandhu, wadakwela kuphili kukapembhela. Wadakhala kumeneko yokha mbaka usiku yapo udajha. 24Ndhawi imeneyo bwato lalikulu lidafika pakatikati pa nyanja, uku nilindengandenga kwa mafunde ndande mbhepo imalibula.
25Mmalenga kucha, Yesu wadaachata oyaluzidwa uku niwayenda pa mwamba pa majhi. 26Oyaluzidwa wake yapo adamwona niwayenda pa mwamba pa majhi, adaopa ni kukamba, “Chimzilimu!” Adabula phokoso ndande ya mandha.
27Nambho pampajha Yesu wadaakambila, “Jhithileni mtima, ni ine. Msadaopa!”
28Petulo wadamkambila, “Ambuye, ngati nde imwe, nikambileni nikuchateni pakuyenda pa mwamba pa majhi.”
29Yesu wadamkambila, “Chabwino, majha.” Ndiipo Petulo wadachika mbwato waukulu, wadayenda pamwamba pa majhi ni kumpitila Yesu. 30Petulo yapo wadawona mbhepo yaikulu, wadaopa ni kuyamba kubila uku niwabula phokoso, “Ambuye, nipulumucheni!”
31Pampajha, Yesu wadatambasula jhanja lake, wadamgwila ni kumkambila, “Iwe wa chikulupi chochepa, ndande yanji uopa?”
32Ndiipo adakwela mbwato waukulu, ni mbhepo nayonjho idasiya. 33Wonjhe adali mbwato waukulu, adagwada ni kumkwatamila, niakamba, “Zenedi iwe ni Mwana wa Mnungu.”
Yesu waalamicha wodwala kumujhi wa Genesaleti
Maluko 6:53-56
34Adayomboka nyanja ni kufika kumujhi wa Genesaleti. 35Wandhu akumeneko yapo adajhiwa kuti ni Yesu, adaziwandicha nghani kumadela yao yonjhe. Wandhu adampelekela Yesu wodwala wao wonjhe, 36adampembha waaloleze wodwala agafye njhonga ya njhalu, ni wonjhe yawo adagafya adalama.
Actualmente seleccionado:
Matayo 14: NTNYBL2025
Destacar
Compartir
Copiar

¿Quieres tener guardados todos tus destacados en todos tus dispositivos? Regístrate o inicia sesión
The New Testament in Nyanja @The Word for The World International and Nyanja Language translation, 2025. All rights reserved.