1
Mateyu 10:16
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
CCL
“Taonani ndikukutumizani inu monga nkhosa pakati pa mimbulu. Chifukwa chake khalani ochenjera ngati njoka ndi woona mtima ngati nkhunda.
Yenzanisa
Ongorora {{vhesi}}
2
Mateyu 10:39
Aliyense amene asunga moyo wake adzawutaya koma aliyense amene ataya moyo chifukwa cha Ine adzawupeza.
3
Mateyu 10:28
Musamaope amene amapha thupi koma sangathe kuchotsa moyo. Koma muziopa Iye amene akhoza kupha mzimu ndi kuwononga thupi mu gehena.
4
Mateyu 10:38
Aliyense amene satenga mtanda wake ndi kunditsata Ine sayenera kukhala wanga.
5
Mateyu 10:32-33
“Aliyense amene avomereza Ine pamaso pa anthu, Inenso ndidzavomereza pamaso pa Atate anga akumwamba. Koma iye amene andikana Ine pamaso pa anthu, Inenso ndidzamukana pamaso pa Atate anga akumwamba.
6
Mateyu 10:8
Chiritsani odwala, ukitsani akufa, chiritsani akhate, tulutsani ziwanda. Munalandira kwaulere, perekani kwaulere.
7
Mateyu 10:31
Potero musaope; inu ndinu a mtengo woposa mbalame zambiri.
8
Mateyu 10:34
“Musaganize kuti Ine ndabweretsa mtendere pa dziko lapansi. Sindinabwere kudzapereka mtendere koma lupanga.