1
Eksodo 28:3
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
CCL
Uwawuze anthu onse aluso amene Ine ndawapatsa nzeru pa ntchito yosoka kuti apange zovala za Aaroni za pa mwambo womupatula, kuti iye anditumikire monga wansembe.
Porównaj
Przeglądaj Eksodo 28:3
2
Eksodo 28:4
Zovala zoti apange ndi izi: chovala chapachifuwa, efodi, mkanjo, mwinjiro wolukidwa, nduwira ndi lamba. Apangire mʼbale wako Aaroni ndi ana ake aamuna zovala zopatulikazi kuti iwo anditumikire monga ansembe.
Przeglądaj Eksodo 28:4