Maluko 15

15
Yesu wapelekedwa pachogolo pa Pilato
Matayo 27:1-2; Luka 23:1-5; Yohana 18:28-38
1Umawamawa, ajhukulu wakulu adachita msonghano ni achogoleli, ni oyaluza thauko, adalamula kumpeleka Yesu kwa Pilato, iye wadali mchogoleli uyo wadachoka ku Loma. Chimwecho adammanga ni kumpeleka kwa Pilato. 2Pilato wadamfunjha Yesu, “Bwanji iwe nde Mfumu wa ayahudi?”
Yesu wadayangha, “Yetu ngati umo iwe ukambila.”
3Ajhukulu wakulu adampacha Yesu mlandu kwa vindhu vambili. 4Pilato wadamfunjhanjho Yesu, “Bwanji siuyangha chalichonjhe? Vechela umo akupachila mlandu kwa vindhu vambili.” 5Nambho Yesu siwadayanghe mawu, chimwecho Pilato wadazizwa.
Yesu walamulidwa kuphedwa
Matayo 27:15-26; Luka 23:13-25; Yohana 18:39; Yohana 19:16
6Kila pwando la Pasaka, pilato wadali ni chikalidwe cha kummasulila mundhu mmojhi wa mndende uyo wamafunika ni wandhu. 7Nyengo imeneyo, kudali ni mundhu mmojhi wamatanidwa Balaba, wadamangidwa pamojhi ni olakwa wina yawo adachita fujho ni kupha. 8Gulu la wandhu ambili adamchata Pilato ni kumpembha wachitile ngati mujha chili chikhalidwe chake. 9Pilato wadaafunjha, “Bwanji, mfuna nimsiilile mfumu wa a Yahudi?” 10Pilato wadakamba chimwecho ndande wadajhiwa kuti wakulu a jhukulu, ampeleka Yesu kwakiye ndande amamuonela njhanje.
11Nambho wakulu a jhukulu adaakhwilizila wandhu ampembhe Pilato wamsiil bile Balaba. 12Pilato wadalifujhanjho, gulu la wandhu, “Chipano mfuna nimchite chiyani mundhu uyu mumtana Mfumu wa a Yahudi?” 13Wadhu wonjhe adakwezanjho mvekelo, “Mpachike pamtanda.” 14Nambho pilato waadafunjha, “Bwanji, walakwa chiyani?”
Nambho anyiiwo adaendekela kubula pokoso kwa mbhavu za mbili, “Mpachike pamtanda.”
15Pilato wadafuna kulikondwelecha gulu la wandhu, chimwecho wadamsiilila Balaba wachoke mndende. Pamenepo wadalamula Yesu wabulidwe mikwapulo, ndiipo ampachike pamtanda.
Asikali amdelela Yesu
Matayo 27:27; Yohana 19:2-3
16Ndiipo anyiwajha asikali adamtenga Yesu adapitanayo kukhomo kwa Pilato, nyumba imeneyo idatanidwa Plaitolio. Mmenemo adakomana asikali ni achanjao wonjhe. 17Adamveka Yesu njhalu ya chifumu, adamkonjela nghata ya minga ni kumveka kumutu. 18Ndiipo adayamba kumlonjela, “Moni Mfumu wa a Yahudi!” 19Adambula ni mkwapulo kumutu, adamlavulila malovu, adamgwadila ni kumlambila. 20Ndiipo yapo adamaliza kumdelela, adamvula ijha njhalu ya chifumu, ni kumveka njhalu zake. Ndiipo adamchocha kubwalo ni kumpachika pamtanda.
Yesu wapachikidwa pamtanda
Matayo 27:32-44; Luka 23:26-43; Yohana 19:17-27
21Yapo adali mnjila, adapezana ni mundhu mmojhi uyo wamatanidwa Simoni, mundhu wa ku Kilene, tate wao Alekizanda ni Lufo. Mundhu mmeneyo wamachokela kumunda wamatopita kumjhini, asikali adamkakamiza wautenge mtanda wa Yesu. 22Ndiipo, adampeleka Yesu mbaka kumalo kumatanidwa Goligota, mate yake, “Pamalo pa fuvu la mutu.” 23Adampacha Yesu divai iyo adasingizana ni mnghwala uwo utanidwa manemane, nambho iye wadakana kuimwa. 24Ndiipo, adampachika Yesu pamtanda, ni kugawana njhalu zake kwa kuzibulila ghudughudu, kuti ajhiwe ghudughudu silimgwele ya ni kuti watenge njhalu. 25Idali saa tatu umawa yapo adampachika Yesu pamtanda. 26Ni mlandu wake udalembedwa chimwechi, “Mfumu wa a Yahudi.” 27Chinchijha Yesu wadapachikidwa pamojhi ni olanda awili pamitanda, mwina kujhanja lake la kwene ni mwina ku jhanja lake la kumanjele. 28Pamenepo yadakwana Malembo Yoyela yayo yalembedwa, “Wadaikidwa pamojhi ni olanda.” #15:28 Bibiliya zina za kale zilibe mzele uwu
29Wandhu amapita pamalo pamenepo amatingiza mitu yao, adamtukwana niakamba, “Iwe udakamba ukhoza kugomola nyumba ya Mnungu ni kuimanganjho siku zitatu! 30Chipano ujhiombole wamwene chika pamtandapo!” 31Chimchijha wakulu wa ajhukulu pamojhi ni oyaluza thauko adampepula Yesu, niakamba, “Wadaombola wandhu ambili nambho siwakhoza kujhiombola mwene! 32Tiyeni timuone kilisito, Mfumu wa a Isilaeli, chipano wachike kuchokela pamtanda, niife sitimkhulupilile.”
Chimchijha wandhu anyiwajha awili adampachikidwa pamojhi ni Yesu adamtukwana.
Yesu wafela pamtanda
Matayo 27:45-56; Luka 23:44-49; Yohana 19:28-30
33Yapo idafika saa sita usana, jhiko lonjhe lidavinikilidwa ni mdima, mdima uwo udakhala kwa masaa ya tatu. 34Saa tisa ujhulo, Yesu wadalila kwa mvekelo waukulu, “Eloi, Eloi, Lema Sabakitani” Mate yake, “Mnungu wanga, Mnungu wanga, ndande yanji mwanisiya?” 35Wandhu wina adaima pajha yapo adavela chimwecho, adakambilana, “Vechelani, wamtana mlosi Eliya.” 36Mundhu mmojhi wadathamanga, ni kubiza buula mu divai yolujhuka, ni wadaika pamwamba pa mkwapulo, ni wadaiika pakamwa pa Yesu niwakamba, “Tilinde tione ngati mlosi Eliya siwajhe kumchicha pamtanda!” 37Yesu wadalila kwa mvekelo, ndiipo wadamwalila.
38Ndiipo panzia ilo lidali pamalo poyela mnyumba ya Mnungu lidang'ambika vidufya viwili kuchokele kumwamba mbaka panjhi. 39Wamkulu mmojhi wa asikali uyo wadaima pachogholo pa mtanda yapo wadaona umo Yesu wadamwalilila, wadakamba, “Zenedi mundhu huyu wadali Mwana wa Mnungu!”
40Pamenepo adalipo wachikazi wina amapenya kwa kutali, pakati pao wadalipo ni Malia wa kumujhi wa Magidala, Salome ni Maliya maye wachi Yakobo wang'ono ni Yusufu. 41Wachikazi achameneo adamchata Yesu yapo wadali ku Galilaya ni kumtumikila. Kudali ni wachikazi wina ambili adajha ku Yelusalemu pamojhi ni iye.
Yesu wazikidwa
Matayo 27:57-61; Luka 23:50-56; Yohana 19:38-42
42Ujhulo yapo udawandikila. Pakuti lidali Siku lo konjekela kupumulila, 43wadajha Yusufu uyo wamachokela ku mujhi wa Alimasaya, mundhu wa bwalo la milandu, wamalemekezeka kupunda wadafika. Mundhu mmeneyo wamalindililila kujha kwa Ufumu wa Mnungu. Chimwecho Yusufu wadampitila Pilato popande kumuopa, wadampembha wampache thupi la Yesu. 44Pilato wadazizwa yapo wadavela kuti Yesu tayali wathomwalila. Ndiipo, wadamtana wamkulu wa asikali ni kumfunjha ngati Yesu wathomwalila. 45Pilato yapo wadakambidwa ni yujha wamkulu wa asikali kuti Yesu wathomwalila, wadamvomeleza Yusufu walitenge thupi la Yesu. 46Yusufu wadaghula sanda, wadalichicha panjhi thupi la Yesu, wadalivilingila sanda. Adaliika pambhanga iyo idakumbidwa pa mwala wolimba. Ndiipo wadaugunghulicha mwala pakhomo pa ijha mbhanga. 47Malia wa ku Magidala ni Maliya make wa Yusufu adapaona pamalo yapo lidaikidwa thupi la Yesu.

Àwon tá yàn lọ́wọ́lọ́wọ́ báyìí:

Maluko 15: NTNYBL2025

Ìsàmì-sí

Pín

Daako

None

Ṣé o fẹ́ fi àwọn ohun pàtàkì pamọ́ sórí gbogbo àwọn ẹ̀rọ rẹ? Wọlé pẹ̀lú àkántì tuntun tàbí wọlé pẹ̀lú àkántì tí tẹ́lẹ̀