Luka Mawu yochogolela

Mawu yochogolela
Chikalakala icha Uthenga Wabwino wa Luka ni chimojhi cha vikalakala vinayi va Chipangano cha Chipano, icho chifotokoza nghani za umoyo wa Yesu Kilisito. Kila chimojhi pakati pa vikalakala ivi chitanidwa chikalakala cha Injili, mawu ili mateyake, Uthenga Wabwino. Vikalakala ivi vidalembedwa ni Matayo, ni Maluko, ni Luka ni Yohana pambuyo kumwalila Yesu. Luka siwadalembe nghani za umoyo wa Yesu pe, nambho wadalembanjho nghani za Yesu ni oyaluzidwa wake adachita ambuyo pa nyifa yake. Wadalembanjho chikalakala icho chiitanidwa Vichito va Atumwi. Palibe uyo wajhiwa nyengo yeneyene iyo Luka wadalemba Uthenga wabwino, ni kapina kuti udalembedwa kuti. Nambho wosoma ambili agwilizana kuti kapina chikalakala chimenecho udalembedwa mchaka cha 70 AD.
Luka, uyo wadalinjho sing'anga, nde uyo wadalemba chikalakala ichi. Mtundu wa kulemba kwake ni mkambo wadaulemba ilangiza kuti Luka ni mundhu uyo wadapita kusukulu. Luka wamafuna kulemba bwino ni kulongosola nghani za umoyo wa Yesu, ni kufotokoza umo vidachitikila vindhu, ni kuti wandhu wina akhoze kupata phindu yapo saoma nghani zimenezo mu Luka 1:1-3. Luka siwadali Myahudi mu Akolosayi 4:10-14, wadalemba chikalakala ichi kwa mtundu uwo wandhu osati Ayahudi akhoza kujhiwa. Nghani izi ziwonekelatu padanga kwa mtundu umo iye wafotokozela mithethe ya Ayahudi mu Luka 1:8.
Uthenga wa Luka ulingana kupunda ni vikalakala va Matayo ni Maluko, ndande vikalakala ivi vifotokoza vindhu vimwevijha kwa mtundu umweujha. Pakati pa vikalakala vitatu, chikalakala cha Luka nde icho chifotokoza bwino nghani za kubadwa kwa Yohana Mbatizi. Luka wadachimikiza kulekeleledwa kwa machimo mu Luka 3:3, 11:4, 17:3-4, 23:34, 24:47 ni wadachimikizanjho mapembhelo mu Luka 3:21, 5:16, 6:12, 11:1-12, 22:32
Yayo yalimo mchikalakala ichi
Mu Luka 1:1-4, Luka waujhiwicha Uthenga wake ni pofotokoza ndande ya kulemba chikalakala ichi.
Ndiipo wafotokoza kuusu kubadwa kwa Yesu ni umo wadajhikonjela kuusu utumiki wake mu Luka 1:5; 4:13
Mmalo yayakulu ya Uthenga yayo yakhalila mu Luka 4:14; 21:38, Luka wafotokoza kuusu njhito izo wadachita Yesu, hasa vodabwicha ivo wadachita ni mayaluzo yayo wadayaluza wandhu.
Pothela, mu sula ziwili zothela, Luka 22:24, Luka wafotokoza umo Yesu wadafela, umo wadazikidwa, ni kuhyukila.

Àwon tá yàn lọ́wọ́lọ́wọ́ báyìí:

Luka Mawu yochogolela: NTNYBL2025

Ìsàmì-sí

Pín

Daako

None

Ṣé o fẹ́ fi àwọn ohun pàtàkì pamọ́ sórí gbogbo àwọn ẹ̀rọ rẹ? Wọlé pẹ̀lú àkántì tuntun tàbí wọlé pẹ̀lú àkántì tí tẹ́lẹ̀