Logo de YouVersion
Icono de búsqueda

Matayo 22

22
Chifani cha chakudya cha ukwati
Luka 14:15-24
1Yesu wadaendekela kukamba nawo kwa chifani. Wadakambila, 2“Ufumu wa kumwamba ulingana ni Mfumu mmojhi uyo wadamkonjela mwana wake wammuna chakudya cha ukwati. 3Wadaatuma mbowa zake wakaatane yao wadalalika ajhe ku ukwati nambho adakana kujha. 4Ndiipo wadaatuma mbowa wina, wadaakambila, ‘Akambileni anyiwajha alalikidwa, naphika chakudya, ng'ombe zanga za mbhongho zazikuluzikulu ni ng'ombe za zing'ono zing'ono zonona zachinjidwa, kila kandhu kali tayali. Majhani mudye!’ 5Nambho wandhu wajha adalalikidwa adadelela, kila mmojhi wadachokapo kupita kunjhito yake, mwina kumunda wake ni mwina kumalonda yake. 6Wina adaagwila mbowa wake, wadaabula ni kwaipha. 7Mfumu mmeneyo wadakwiya kupunda, chimwecho wadaatuma asikali wake wakaaphe wandhu wajha wadaapha mbowa zake ni kuipyeleza mijhi yao. 8Ndiipo wadaatana mbowa zake ni kwaakambila, ‘Phwando la ukwati lali tayali, nambho anyiyao naalalika siadakwanile kujha kuphwando. 9Chimwecho pitani mmikwakwa ya mijhi ni walionjhe uyo simumuone, mlalikeni wajhe kupwando la ukwati.’ 10Mbowa wajha adapita mnjila za mmikwakwa, wadatana wandhu wonjhe yawo adadulichana, oyipa ni abwino. Phwando lidajhala alendo. Mnyumba mujha mdachitikila ukwati mdajhala alendo.”
11“Mfumu yapo wadalowa mkati wadapenya alendo wake, wadaona muli mundhu siwadavale njhalu ya ukwati. 12Mfumu wadamfunjha, ‘Bwenji, walowa bwanji malo yano popande kuvala njhalu ya ukwati?’ Nambho mundhu yujha siwadayanghe. 13Pamenepo mfumu wadaakambila mbowa ‘Mmangeni myendo ni mmanjha mkamponye kubwalo kumdima. Kumeneko siwalile ni kubukutula mano.’”
14Yesu wadamaliza kwa kukamba, “Wandhu yawo alalikidwa ni ambili, nambho yawo asanghidwa ni ochepa.”
Nghani yolipila msongho
Maluko 12:13-17; Luka 20:20-26
15Ndiipo Afalisayo adachoka ni adafunafuna njila ya kumgwila Yesu kwa mawu yake. 16Adaatuma oyaluzidwa wao pamojhi ni wandhu agulu la Helode. Adakamba, “Oyaluza, tijhiwa kuti iwe ni mzene ni uyaluza mau la Amnungu kwa uzene, ndande siuopa ukulu wa mundhu. 17Tikambile chipano, uona bwanji ife tifunika kulipa msongho kwa mfumu wa ku Loma kapina notho?”
18Nambho Yesu wadajhiwa voipa vao wadakamba, “Agunghuli anyiimwe, ndande yanji munichela? 19Nilangizeni gelenjha la ndalama iyo mlipila msongho!”
Anyiiwo adampelekela gelenjha la ndalama. 20Ndiipo Yesu wadafunjha, “Bwanji, nghope ni jhina ili ni vayani?”
21Adamuyangha, “Va mfumu wa ku Loma,”
Pamwepo Yesu wadakambila, “Va mfumu wa ku Loma mpacheni mfumu wa ku Loma ni va Amnungu mpacheni Mnungu.”
22Yapo adavela chimwecho adadabwa, chimwecho adamsiya ni kuchoka.
Asadukayo amfunjha Yesu nghani za kuhyuka
Maluko 12:18-27; Luka 20:27-40
23Siku limwelo akumojhi wa Asadukayo, yawo akamba, palibe kuhyuka kwa wandhu, adampitila Yesu, adamkambila, 24“Oyaluza, Musa wadakamba ngati mundhu wammuna wamwalila popande kusiya mwana, mbale wake wamkwate wamkazi wafedwa ni mmunake kuti wambalile mbalewake wana. 25Pano pathu padali ni abale saba. Oyamba wadakwata ni kumwalila, ndande wadalibe mwana, mpwake wadalowa chokolo wamkazi mmeneyo. 26Chindhu chimchijha chidamchitikila mbale wa kawili ni waka tatu mbaka wa saba. 27Pothela wamkazi mmeneyo nayo wadamwalila. 28Akahyuka wamkazi siwakhale wayani pakuti wonjhe saba adamkwata.”
29Yesu wadayangha wajha Asadukayo, “Mwasokelela anyiimwe, pakuti simujhiwa malembo yoyela kapina mbhavu za Mnungu. 30Wandhu yapo ahyuka palibe kukwata kapena kukwatiwa, siakhale ngati mtumiki wa kumwamba. 31Pa nghani za kuhyuka, simdajhiwe chijha wadakukambilani Mnungu? Wadaakambila, 32‘Ine nde Mnungu wa Ibulahimu ni Mnungu wa Isaka ni Mnungu wa Yakobo.’ Chimwecho, Mnungu osati Mnungu wa wandhu omwalila, nambho ni Mnungu wa wandhu amoyo.”
33Gulu la wandhu yapo lidavela mawu yameneyo lidazizwa mayaluzo yake.
Lamulo lalikulu
Maluko 12:28-34; Luka 10:25-28
34Afalisayo yapo adavela Yesu waachita masadukayo akhale chete, adakomana pamojhi. 35Mmojhi wao wa oyaluza thauko wadamfunjha Yesu kwa kumchela, 36“Oyaluza, pamathauko yonjhe thauko liti lili lalikulu?”
37Yesu wadamuyangha, “Mkonde Ambuye Mnungu wako kwa mtima wako onjhe ni mzimu wako onjhe ni njelu zako zonjhe. 38Ili nde lamulo lalikulu ni loyamba. 39Lamulo la kawili lilingana ni ili, ‘Mkonde mnjako ngati umo ujhikondela umwene wake.’ 40Pamathuko yonjhe ni mayaluzo ya alosi, yonjhe yachokana ni malamulo yaya yawili.”
Kilisito ni yani
Maluko 12:35-37; Luka 20:41-44
41Afalisayo wajha yapo adali akomana pamojhi pampajha, Yesu wadaafunjha, 42wadaakambila, “Bwanji, anyiimwe mganiza kuti Kilisito muomboli ni mwana wa yani?”
Adamuyangha, “Wa Daudi,”
43Yesu wadaafunjha, “Ndande yanji Mzimu Woyela umchogoza Daudi wamtane ‘Mbuye?’ pakuti Daudi wadakamba,
44‘Ambuye adaakambila Mmbuye wanga,
Khala jhanja langa la kwene,
mbaka naike adani wako panjhi pa myendo yako mbaka yapo siwakhoze adani wako wonjhe.’
45Ngati Daudi watana Kilisito, ‘Ambuye,’ ikhala bwanji Kilisito wakhale mwana wa Daudi?”
46Palibe uyo wadayangha mau. Kuchokela siku limenelo ni kuyendekela palibe uyo wadayesa kumfunjha Yesu.

Actualmente seleccionado:

Matayo 22: NTNYBL2025

Destacar

Compartir

Copiar

None

¿Quieres tener guardados todos tus destacados en todos tus dispositivos? Regístrate o inicia sesión