Maluko 6
6
Wandhu a ku Nazaleti amkana Yesu
Matayo 13:53-58; Luka 4:16-30
1Yesu wadachoka pamenepo ni kupita ku mujhi wa ku Nazaleti kumalo uku wadakulila, ni oyaluzidwa wake adamchata. 2Siku lo Pumulila yapo lidafika, wadayamba kuyaluza mnyumba yokomanilana Ayahudi. Wandhu ambili yawo adamvela adazizwa kupunda ni adajhifunjha, “Bwanji, wayapata kuti mayaluzo yaya? Ekima yanji walinayo mbaka wachita vindu vodabwicha? 3Uyu osati yujha wosepa mitengo, mwana wa Maliya ni achabale wake ni achi yakobo, ni Yusufu ni Yuda ni Simoni? Bwanji, achalongo wake siali pano ni ife?” Nianyiiwo adaipila kupunda ni, adamkana kumkhulupilila.
4Yesu wadaakambila, “Alosi alemekezedwa kumalo konjhe, nambho saalemekezedwa ni wandhu amnyumba zawo, ni mmijhi yawo ni kwa achaabale wao.”
5Yesu siwadafune kuchita vodabwicha kumeneko, nambho wadaaikila manja odwala ochepa ni kwalamicha. 6Yesu wadazizwa kupunda ndande ya kosakhulupilile kwawo.
Yesu waatuma woyaluzidwa khumi ni awili
Matayo 10:5-15; Luka 9:1-6
Yesu wamaviyendela vijhivjhi vapafupi ni pajha, niwaayaluza wandhu. 7Wadaatana wajha oyaluzidwa khumi ni awili, wadapacha ulamulilo wotopola viwanda, ni kwaatuma awiliawili. 8Wadaalamula, “Simdatenga chindhu chalichonjhe ndande ya ulendo, nambho mtenge mpulupe. Simdatenga chakudya kapina thumba, kapina ndalama pachilolo. 9Valani malapasi, nambho msidatenga njhalu zo ng'anamula.” 10Chinchijha wadaakambila, “Panyumba paliponjhe yapo siakulandileni, mkhale pamenemo mbaka yapo simuchoke. 11Pamalo paliponjhe, wandhu yapo saakane kukulandilani ni kukuvechelani, chokani pamalo pamenepo ni kukung'undha lifumbi ilo lakhalila mmyendo mwanu kulangiza kuti asangha kukana kuulandila Uthenga wa Mnungu.” 12Chimwecho, adachoka, ni kupita kwaalalikila wandhu alape. 13Amaachocha wandhu viwanda vambili, ni adaanyeka mafuta odwala ambili, ni kwalamicha.
Kumwalila kwa Yohana Mbatizi
Matayo 14:1-12; Luka 9:7-9
14Ndiipo, mfumu Helode wadavela nghani zimenezo zonjhe, pakuti Yesu wadajhiwika kumalo konjhe. Wandhu wonjhe adakamba, “Yohana Mbatizi wahyuka, wali ni mbhavu zochita vodabwicha ndande ni mlosi.” 15Nambho wandhu wina adakamba, “Uyu ni mlosi Eliya.” Wina adakamba “Uyu ni mmojhi wa alosi akale.”
16Nambho Helode yapo wadapata nghani zimenezo, wadakamba, “Uyu ni Yohana Mbatizi, uyo nidamdula mutu, wahyuka.”
17Helode mwene wake wadalamula Yohana wagwilidwe, waikidwe mndende. Helode wadachita chimwecho ndande ya Helodia uyo wadamkwata, wamkazi mmeneyo wadali wamkazi wa Filipo mphwake wa Helode. 18Helode wadamchitila chimwecho Yohana ndande wadamkambila, “Osati bwino iwe kumkwata wamkazi wa mphwako!”
19Pamenepo Helodia wadamuipila kupunda Yohana, wamafuna kumpha, nambho siwadakhoze, 20ndande Helode wamamlonda. Helode wamamuopa Yohana pakuti wadajhiwa kuti wadali mundhu wabwino pamaso pa Mnungu, chimwecho wamamsunga. Helode wamakonda kumvechela Yohana, ingakhale wamavutika kupunda yapo wamamaliza kumvechela.
21Siku limojhi Helodia wadapata malo ya kumpha Yohana pa phwando lakubadwa kwa Helode. Helode wadaachitila phwando lalikulu mbowa zake, wakuluakulu asikali ni achogoleli aku jhiko la Galilaya. 22Mwali wa Helodia yapo wadalowa pamalo pajha amachitila pwando, wadavina, wadamkondwelecha kupunda Helode ni alendo wake. Chimwecho mfumu Helode wadamkambila yujha mwali, “Pembha chalichonjhe icho ufuna, nane sinikupache.” 23Wadalumbila, “Sinikupache chilichonjhe icho siunipembhe, ine sinikupache, ata ngati nusu ya ufumu wanga sinikupache.”
24Pamenepo yujha mwali wadachoka, ni kupita kwafunjha maye wake, “Nipembhe chiyani?”
Nawo wajha amake adamuyangha “Pembha mutu wa Yohana Mbatizi.” 25Yujha mwali wadathamanga mbaka kwa mfumu nikumpembha, “Nipembha mnipache saino muliselo mutu wa Yohana Mbatizi.”
26Mfumu wadaona chisoni kupunda, nambho siwadakhoze kukana, ndande wadalumbila pachogolo pa alendo wake. 27Pampajha mfumu wadamkambila asikali wajhe nawo mutu wa Yohana Mbatizi mliselo. Asikali uyo wadapita mndende, wadamdula mutu Yohana. 28Ndiipo yujha asikali wadajhanawo mutu mliselo ni kumpacha mwali, ni iye mwali wadapacha amake. 29Oyaluzidwa a Yohana yapo adavela nghani imeneyo, adapita kulitenga thupi la Yohana ni kulizika.
Yesu waapacha chakudya wandhu elufu zisano
Matayo 14:13-21; Luka 9:10-17; Yohana 6:1-14
30Anyiwajha atumwi adabwela kuchokela uko adatumidwa, ni adasonghana pachogolo pa Yesu, niadamkambila yonjhe yayo adayachita ni yajha amayaluza. 31Yesu wadaakambila, “Tiyeni ife tekha pamalo yapo palibe wandhu, kuti tikapumulile pang'ono.” Wadakamba chimwecho ndande kudali ni wandhu ambili kupunda yawo amajha pamenepo ni kuchoka, mbaka Yesu ni oyaluzidwa wake siamakhoze kupata ndhawi ya kudya chakudya ndande ya kwatumikila. 32Ndiipo, adachoka okha kwa boti ni kupita kumalo yapo padalibe wandhu.
33Nambho wandhu ambili yapo wadaona niachoka, adajhiwa uko apita. Chimwecho, wandhu ambili adachokela mmijhi yosiyanasiyana, adathamanga ni kwachogolela kufika. 34Yesu yapo wadachika mboti, wadaliona gulu lalikulu la wandhu, wadaalengela lisungu ndande adali ngati mbelele zilibe owesa. Chimwecho wadayamba kwayaluza vindhu vambili. 35Ujhulo yapo udajha, oyaluzidwa adamchata Yesu, adamkambila, “Pamalo pano ni paphululu, ni jhuwa litobila. 36Waakambile wandhu apite mminda ni mvijhijhi va pafupi akajhigulile chakudya.” 37Nambho Yesu wadaakambila, “Mwachinawene wake mwapache chakudya.” Ni anyiiyo adamfunjha, “Bwanji, tipite kugula mabumunda ya dinali miyambili ni kwapacha wandhu adye?” 38Yesu waadafunjha, “Mli ni mabumunda yangati? Pitani mkapenye, mkaiwelenge.” Yapo adawelenga, adamkambila, “Yalipo mabumunda yasano ni njhomba ziwili.”
39Ndiipo, Yesu wadaakambila oyaluzidwa wake, waakambile wandhu akhale magulu mgulu pamachamba yayawisi. 40Chimwecho adakhala magulu ya wandhu miya ni ya wandhu amsini. 41Ndiipo, Yesu wadayatenga yajha mabumunda yasano ni zijha njhomba ziwili, wadapenya kumwamba, wadamuyamika Mnungu, ndiipo wadayadula yajha mabumunda. Wadaapacha oyaluzidwa wake kuti wagawile wandhu. Chinchijha wadagawila wandhu zijha njhomba ziwili. 42Wandhu wonjhe adadya ni kukhuta. 43Ndiipo oyaluzidwa wake adatondola vidufya va mabumunda ni njhomba ivo vidakhalila, ni adajhaza miseche khumi ni iwili. 44Wachimunape yawo adadya yajha mabumunda adali ngati elufu zisano.
Yesu wayenda pamwamba pa majhi
Matayo 14:22-33; Yohana 6:15-21
45Pamwepo Yesu wadaalamula oyaluzidwa wake akwele mboti, amchogolele kupita ku kuchidya kwa nyanja mbaka Ku Betisaida, iye wamalilaila gulu la wandhu. 46Yapo wadamaliza kwalaila wandhu, wadapita kuphili kupembhela. 47Usiku yapo udalowa, lijha boti lidali pakatikati pa nyanja, Yesu wadali yokha pamtunda. 48Ndiipo, Yesu wadaaona oyaluzidwa wake niavutika kwa kupalasa nghafi, ndande mbhepo imaabula kwa mbhavu. Mmalengakucha, Yesu wadayendela oyaluzidwa wake uku niwayenda pamwamba pa majhi, wamafuna kwapitilila. 49Yapo adamwona ni wayenda pamwamba pa majhi, amaganizila udali mzilimu, adabula pokhoso. 50Pakuti wonjhe adamwona, ni adaopa. Yesu wadaakambila, “Jhitileni mtima! Ni ine! Msadaopa!” 51Ndiipo wadakwela mboti umo adali woyaluzidwa, ni mbhepo idasiya, oyaluzidwa wake adazizwa kupunda, 52adali akali osajhiwe vodabwicha va mabumunda, ndande mitima yao idali yopapatala kukhulupilila.
Yesu waalamicha wodwala ku Genesaleti
Matayo 14:34-36
53Adayomboka nyanja ni kufika mjhiko la Genesaleti, ni kutaya ndondowe. 54Yapo adachika mboti, pampajha wandhu adamjhiwa Yesu. 55Ndiipo, kwa chisanga adazungulila mjhiko lonjhe, adayamba kwatenga wodwala pa vitala vawo, ni kwapeleka kumalo kujha adavela Yesu walipo. 56Mmalo yonjhe yayo Yesu wamapita, mmijhi ni mvijhijhi kapina mmalo yonjhe. Wandhu amaika odwala paliwala, adampembha ata ngati amgwile njhalu zake, niwonjhe yawo adagafya njhonga ya njhalu yake adalama.
നിലവിൽ തിരഞ്ഞെടുത്തിരിക്കുന്നു:
Maluko 6: NTNYBL2025
ഹൈലൈറ്റ് ചെയ്യുക
പങ്ക് വെക്കു
പകർത്തുക

നിങ്ങളുടെ എല്ലാ ഉപകരണങ്ങളിലും ഹൈലൈറ്റുകൾ സംരക്ഷിക്കാൻ ആഗ്രഹിക്കുന്നുണ്ടോ? സൈൻ അപ്പ് ചെയ്യുക അല്ലെങ്കിൽ സൈൻ ഇൻ ചെയ്യുക
The New Testament in Nyanja @The Word for The World International and Nyanja Language translation, 2025. All rights reserved.
Maluko 6
6
Wandhu a ku Nazaleti amkana Yesu
Matayo 13:53-58; Luka 4:16-30
1Yesu wadachoka pamenepo ni kupita ku mujhi wa ku Nazaleti kumalo uku wadakulila, ni oyaluzidwa wake adamchata. 2Siku lo Pumulila yapo lidafika, wadayamba kuyaluza mnyumba yokomanilana Ayahudi. Wandhu ambili yawo adamvela adazizwa kupunda ni adajhifunjha, “Bwanji, wayapata kuti mayaluzo yaya? Ekima yanji walinayo mbaka wachita vindu vodabwicha? 3Uyu osati yujha wosepa mitengo, mwana wa Maliya ni achabale wake ni achi yakobo, ni Yusufu ni Yuda ni Simoni? Bwanji, achalongo wake siali pano ni ife?” Nianyiiwo adaipila kupunda ni, adamkana kumkhulupilila.
4Yesu wadaakambila, “Alosi alemekezedwa kumalo konjhe, nambho saalemekezedwa ni wandhu amnyumba zawo, ni mmijhi yawo ni kwa achaabale wao.”
5Yesu siwadafune kuchita vodabwicha kumeneko, nambho wadaaikila manja odwala ochepa ni kwalamicha. 6Yesu wadazizwa kupunda ndande ya kosakhulupilile kwawo.
Yesu waatuma woyaluzidwa khumi ni awili
Matayo 10:5-15; Luka 9:1-6
Yesu wamaviyendela vijhivjhi vapafupi ni pajha, niwaayaluza wandhu. 7Wadaatana wajha oyaluzidwa khumi ni awili, wadapacha ulamulilo wotopola viwanda, ni kwaatuma awiliawili. 8Wadaalamula, “Simdatenga chindhu chalichonjhe ndande ya ulendo, nambho mtenge mpulupe. Simdatenga chakudya kapina thumba, kapina ndalama pachilolo. 9Valani malapasi, nambho msidatenga njhalu zo ng'anamula.” 10Chinchijha wadaakambila, “Panyumba paliponjhe yapo siakulandileni, mkhale pamenemo mbaka yapo simuchoke. 11Pamalo paliponjhe, wandhu yapo saakane kukulandilani ni kukuvechelani, chokani pamalo pamenepo ni kukung'undha lifumbi ilo lakhalila mmyendo mwanu kulangiza kuti asangha kukana kuulandila Uthenga wa Mnungu.” 12Chimwecho, adachoka, ni kupita kwaalalikila wandhu alape. 13Amaachocha wandhu viwanda vambili, ni adaanyeka mafuta odwala ambili, ni kwalamicha.
Kumwalila kwa Yohana Mbatizi
Matayo 14:1-12; Luka 9:7-9
14Ndiipo, mfumu Helode wadavela nghani zimenezo zonjhe, pakuti Yesu wadajhiwika kumalo konjhe. Wandhu wonjhe adakamba, “Yohana Mbatizi wahyuka, wali ni mbhavu zochita vodabwicha ndande ni mlosi.” 15Nambho wandhu wina adakamba, “Uyu ni mlosi Eliya.” Wina adakamba “Uyu ni mmojhi wa alosi akale.”
16Nambho Helode yapo wadapata nghani zimenezo, wadakamba, “Uyu ni Yohana Mbatizi, uyo nidamdula mutu, wahyuka.”
17Helode mwene wake wadalamula Yohana wagwilidwe, waikidwe mndende. Helode wadachita chimwecho ndande ya Helodia uyo wadamkwata, wamkazi mmeneyo wadali wamkazi wa Filipo mphwake wa Helode. 18Helode wadamchitila chimwecho Yohana ndande wadamkambila, “Osati bwino iwe kumkwata wamkazi wa mphwako!”
19Pamenepo Helodia wadamuipila kupunda Yohana, wamafuna kumpha, nambho siwadakhoze, 20ndande Helode wamamlonda. Helode wamamuopa Yohana pakuti wadajhiwa kuti wadali mundhu wabwino pamaso pa Mnungu, chimwecho wamamsunga. Helode wamakonda kumvechela Yohana, ingakhale wamavutika kupunda yapo wamamaliza kumvechela.
21Siku limojhi Helodia wadapata malo ya kumpha Yohana pa phwando lakubadwa kwa Helode. Helode wadaachitila phwando lalikulu mbowa zake, wakuluakulu asikali ni achogoleli aku jhiko la Galilaya. 22Mwali wa Helodia yapo wadalowa pamalo pajha amachitila pwando, wadavina, wadamkondwelecha kupunda Helode ni alendo wake. Chimwecho mfumu Helode wadamkambila yujha mwali, “Pembha chalichonjhe icho ufuna, nane sinikupache.” 23Wadalumbila, “Sinikupache chilichonjhe icho siunipembhe, ine sinikupache, ata ngati nusu ya ufumu wanga sinikupache.”
24Pamenepo yujha mwali wadachoka, ni kupita kwafunjha maye wake, “Nipembhe chiyani?”
Nawo wajha amake adamuyangha “Pembha mutu wa Yohana Mbatizi.” 25Yujha mwali wadathamanga mbaka kwa mfumu nikumpembha, “Nipembha mnipache saino muliselo mutu wa Yohana Mbatizi.”
26Mfumu wadaona chisoni kupunda, nambho siwadakhoze kukana, ndande wadalumbila pachogolo pa alendo wake. 27Pampajha mfumu wadamkambila asikali wajhe nawo mutu wa Yohana Mbatizi mliselo. Asikali uyo wadapita mndende, wadamdula mutu Yohana. 28Ndiipo yujha asikali wadajhanawo mutu mliselo ni kumpacha mwali, ni iye mwali wadapacha amake. 29Oyaluzidwa a Yohana yapo adavela nghani imeneyo, adapita kulitenga thupi la Yohana ni kulizika.
Yesu waapacha chakudya wandhu elufu zisano
Matayo 14:13-21; Luka 9:10-17; Yohana 6:1-14
30Anyiwajha atumwi adabwela kuchokela uko adatumidwa, ni adasonghana pachogolo pa Yesu, niadamkambila yonjhe yayo adayachita ni yajha amayaluza. 31Yesu wadaakambila, “Tiyeni ife tekha pamalo yapo palibe wandhu, kuti tikapumulile pang'ono.” Wadakamba chimwecho ndande kudali ni wandhu ambili kupunda yawo amajha pamenepo ni kuchoka, mbaka Yesu ni oyaluzidwa wake siamakhoze kupata ndhawi ya kudya chakudya ndande ya kwatumikila. 32Ndiipo, adachoka okha kwa boti ni kupita kumalo yapo padalibe wandhu.
33Nambho wandhu ambili yapo wadaona niachoka, adajhiwa uko apita. Chimwecho, wandhu ambili adachokela mmijhi yosiyanasiyana, adathamanga ni kwachogolela kufika. 34Yesu yapo wadachika mboti, wadaliona gulu lalikulu la wandhu, wadaalengela lisungu ndande adali ngati mbelele zilibe owesa. Chimwecho wadayamba kwayaluza vindhu vambili. 35Ujhulo yapo udajha, oyaluzidwa adamchata Yesu, adamkambila, “Pamalo pano ni paphululu, ni jhuwa litobila. 36Waakambile wandhu apite mminda ni mvijhijhi va pafupi akajhigulile chakudya.” 37Nambho Yesu wadaakambila, “Mwachinawene wake mwapache chakudya.” Ni anyiiyo adamfunjha, “Bwanji, tipite kugula mabumunda ya dinali miyambili ni kwapacha wandhu adye?” 38Yesu waadafunjha, “Mli ni mabumunda yangati? Pitani mkapenye, mkaiwelenge.” Yapo adawelenga, adamkambila, “Yalipo mabumunda yasano ni njhomba ziwili.”
39Ndiipo, Yesu wadaakambila oyaluzidwa wake, waakambile wandhu akhale magulu mgulu pamachamba yayawisi. 40Chimwecho adakhala magulu ya wandhu miya ni ya wandhu amsini. 41Ndiipo, Yesu wadayatenga yajha mabumunda yasano ni zijha njhomba ziwili, wadapenya kumwamba, wadamuyamika Mnungu, ndiipo wadayadula yajha mabumunda. Wadaapacha oyaluzidwa wake kuti wagawile wandhu. Chinchijha wadagawila wandhu zijha njhomba ziwili. 42Wandhu wonjhe adadya ni kukhuta. 43Ndiipo oyaluzidwa wake adatondola vidufya va mabumunda ni njhomba ivo vidakhalila, ni adajhaza miseche khumi ni iwili. 44Wachimunape yawo adadya yajha mabumunda adali ngati elufu zisano.
Yesu wayenda pamwamba pa majhi
Matayo 14:22-33; Yohana 6:15-21
45Pamwepo Yesu wadaalamula oyaluzidwa wake akwele mboti, amchogolele kupita ku kuchidya kwa nyanja mbaka Ku Betisaida, iye wamalilaila gulu la wandhu. 46Yapo wadamaliza kwalaila wandhu, wadapita kuphili kupembhela. 47Usiku yapo udalowa, lijha boti lidali pakatikati pa nyanja, Yesu wadali yokha pamtunda. 48Ndiipo, Yesu wadaaona oyaluzidwa wake niavutika kwa kupalasa nghafi, ndande mbhepo imaabula kwa mbhavu. Mmalengakucha, Yesu wadayendela oyaluzidwa wake uku niwayenda pamwamba pa majhi, wamafuna kwapitilila. 49Yapo adamwona ni wayenda pamwamba pa majhi, amaganizila udali mzilimu, adabula pokhoso. 50Pakuti wonjhe adamwona, ni adaopa. Yesu wadaakambila, “Jhitileni mtima! Ni ine! Msadaopa!” 51Ndiipo wadakwela mboti umo adali woyaluzidwa, ni mbhepo idasiya, oyaluzidwa wake adazizwa kupunda, 52adali akali osajhiwe vodabwicha va mabumunda, ndande mitima yao idali yopapatala kukhulupilila.
Yesu waalamicha wodwala ku Genesaleti
Matayo 14:34-36
53Adayomboka nyanja ni kufika mjhiko la Genesaleti, ni kutaya ndondowe. 54Yapo adachika mboti, pampajha wandhu adamjhiwa Yesu. 55Ndiipo, kwa chisanga adazungulila mjhiko lonjhe, adayamba kwatenga wodwala pa vitala vawo, ni kwapeleka kumalo kujha adavela Yesu walipo. 56Mmalo yonjhe yayo Yesu wamapita, mmijhi ni mvijhijhi kapina mmalo yonjhe. Wandhu amaika odwala paliwala, adampembha ata ngati amgwile njhalu zake, niwonjhe yawo adagafya njhonga ya njhalu yake adalama.
നിലവിൽ തിരഞ്ഞെടുത്തിരിക്കുന്നു:
:
ഹൈലൈറ്റ് ചെയ്യുക
പങ്ക് വെക്കു
പകർത്തുക

നിങ്ങളുടെ എല്ലാ ഉപകരണങ്ങളിലും ഹൈലൈറ്റുകൾ സംരക്ഷിക്കാൻ ആഗ്രഹിക്കുന്നുണ്ടോ? സൈൻ അപ്പ് ചെയ്യുക അല്ലെങ്കിൽ സൈൻ ഇൻ ചെയ്യുക
The New Testament in Nyanja @The Word for The World International and Nyanja Language translation, 2025. All rights reserved.