1
LUKA 9:23
Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014
BLPB2014
Ndipo Iye ananena kwa onse, Ngati munthu afuna kudza pambuyo panga, adzikanize yekha, nanyamule mtanda wake tsiku ndi tsiku, nanditsate Ine.
Konpare
Eksplore LUKA 9:23
2
LUKA 9:24
Pakuti amene aliyense akafuna kupulumutsa moyo wake, iye adzautaya; koma amene aliyense akataya moyo wake chifukwa cha Ine, iye adzaupulumutsa uwu.
Eksplore LUKA 9:24
3
LUKA 9:62
Koma Yesu anati kwa iye, Palibe munthu wakugwira chikhasu, nayang'ana za kumbuyo, ayenera Ufumu wa Mulungu.
Eksplore LUKA 9:62
4
LUKA 9:25
Pakuti munthu apindulanji, akadzilemezera dziko lonse lapansi nadzitayapo, kapena kulipapo moyo wake?
Eksplore LUKA 9:25
5
LUKA 9:26
Pakuti amene aliyense adzachita manyazi chifukwa cha Ine ndi mau anga, Mwana wa Munthu adzachita manyazi chifukwa cha iye, pamene adzafika ndi ulemerero wake ndi wa Atate, ndi wa angelo oyera.
Eksplore LUKA 9:26
6
LUKA 9:58
Ndipo Yesu anati kwa iye, Nkhandwe zili nazo nkhwimba, ndi mbalame za kumwamba zisa, koma Mwana wa Munthu alibe potsamira mutu.
Eksplore LUKA 9:58
7
LUKA 9:48
Amene aliyense akalandire kamwana aka m'dzina langa alandira Ine; ndipo amene andilandira Ine alandira Iye amene anandituma Ine; pakuti iye wakukhala wamng'onong'ono wa inu nonse, yemweyu ndiye wamkulu.
Eksplore LUKA 9:48
Akèy
Bib
Plan yo
Videyo