1
Yohane 1:12
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
CCL
Koma kwa onse amene anamulandira Iye, kwa amene anakhulupirira mʼdzina lake, Iye anawapatsa mphamvu yokhala ana a Mulungu
Yenzanisa
Ongorora {{vhesi}}
2
Yohane 1:1
Pachiyambi panali Mawu, ndipo Mawu anali kwa Mulungu, ndipo Mawu ndiye Mulungu.
3
Yohane 1:5
Kuwunika kunawala mu mdima, koma mdimawo sunakuzindikire.
4
Yohane 1:14
Mawu anasandulika thupi ndipo anakhala pakati pathu. Ife tinaona ulemerero wake, ulemerero wa Iye amene ndi Mwana mmodzi yekhayo wa Atate, wodzaza ndi chisomo ndi choonadi.
5
Yohane 1:3-4
Zinthu zonse zinalengedwa ndi Iye; ndipo popanda Iye sikukanakhala kanthu kalikonse kolengedwa. Mwa Iye munali moyo, ndipo moyowo unali kuwunika kwa anthu.
6
Yohane 1:29
Pa tsiku lotsatira Yohane anaona Yesu akubwera kwa iye ndipo anati, “Taonani, Mwana Wankhosa wa Mulungu, amene achotsa tchimo la dziko lapansi!
7
Yohane 1:10-11
Iye anali mʼdziko lapansi, ndipo ngakhale kuti dziko lapansi linalengedwa ndi Iye, dziko lapansilo silinamuzindikire Iye. Iye anabwera kwa iwo amene anali akeake, koma akewo sanamulandire Iye.
8
Yohane 1:9
Kuwunika koona kumene kuwunikira munthu aliyense kunabwera ku dziko lapansi.
9
Yohane 1:17
Pakuti lamulo linapatsidwa kudzera mwa Mose; chisomo ndi choonadi zinabwera kudzera mwa Yesu Khristu.
Pekutangira
Bhaibheri
Zvirongwa
Mavideo