Vichito 10
10
Petulo wamuyendela Konelio
1Kudali mundhu mmojhi mu Kaisaliya jhina lake Konelio, uyo wadali wamkulu wa gulu la nghondo mia mojha ilo lidatanidwa, Gulu la Kiitaliya. 2Iye pamojhi ni nyumba yake adali wandhu womlambila Mnungu. Iye wadalinjho mundhu wothangatila Ayahudi wosauka ni kumpembha Mnungu popande kuleka. 3Siku limojhi ndhawi ya saa tisa usana, iye wadaona masombhenya waziwazi, mtumiki wa kumwamba wa Mnungu niwajhela, wadakamba, “Konelio!”
4Konelio wadampenyechecha mtumiki wa kumwamba wa Mnungu kwa mandha ni kukamba, “Kulichiyani Ambuye?”
Yujha mtumiki wadamuyanghga, “Mnungu wayavela mapembhelo yako ni kuziona njhembe zako izo waapacha wandhu osauka ni saaziyawalila. 5Chipano umtume mthenga wapite ku Yopa, wakamtane Simoni uyo watanidwa Petulo. 6Iye ni mlendo wa Simoni uyo wakonja vikwetu, Nyumba yake ili pafupi ni nyanja ya mchele.” 7Ndiipo yujha mtumiki wa Mnungu wa kumwamba wamakambanayo, yapo wadachoka, Konelio wadaatana mbowa wake awili pamojhi ni asikali mmojhi kukhomo lake, uyo wamlambila Mnungu kwa uzene. 8Konelio wadaakambila yayo yadachitika ni kwaatuma kupita ku Yopa.
9Siku la kawili lake, wandhu wajha atatu yapo adali mnjila naawandikila pa mujhi wa Yopa, Petulo wadakwela pa chindu la nyumba ndhawi ya saa sita usana kuti wapembhele. 10Wadaona njala ni wadakhumbila kudya chakudya. Nambho yapo amakonja chakudya, iye wadagona litulo ni kuona masombhenya. 11Wadaona kumwamba kwachekuka, ni chindhu icho chidali ngatinjhalu yaikulu chidachichidwa panjhi uku chagwilidwa njhonga zake zinayi. 12Mkati mwake mudali mitundu yonjhe ya zinyama, zokwawa ni mbalame. 13Wadavela mvekelo, “Ima Petulo, uphe ni kudya!”
14Nambho Petulo wadakamba, “Notho Ambuye! Sinidadyepo chakudya chilichonjhe icho chakanizidwa kudyedwa kapina icho sichivomelezeka pakumlambila Mnungu.”
15Ujha mvekelo udavekanjho, “Vindhu ivo vavomelezedwa ni Mnungu kudyedwa siudavitana vindhu ivo sivifunika.” 16Chindhu ichi cha kumkambila Petulo ipha ni udye wadakambidwa mala katatu, ndiipo chindhu chijha chidali ngati njhalu yaikulu chidatengedwa kupita kumwamba.
17Petulo yapo wadali wakali kujhifunjha mafunjho ya yajha masombhenya, wandhu adatumidwa ni Koneliya, yapo adaijhiwa nyumba ya Simoni wokonja vikwetu, adafika ni kuima pachicheko. 18Adagogoda ni kufunjha, “Bwanji, pali mlendo pano jhina lake Simoni uyo wamatanidwa Simoni Petulo?”
19Petulo wamaganizila yajha masombhenya, Mzimu Woyela udamkambila, “Simoni, pali wandhu atatu pano akufuna iwe. 20Chika panjhi chisanga, ni usadakhaikila kupita nawo, pakuti ine nde naatuma.” 21Chimwecho Petulo wadachika ni nikwaakambila wandhu wajha, “Ine nde mundhu uyo mumfuna. Mwachata chiyani pano?”
22Wandhu wajha adamuyangha, “Tatumidwa ni wamkulu wa asikali uyo watanidwa Konelio. Iye ni mundhu wabwino uyo wamamkonda Mnungu ni kulemekezeka ni Ayahudi wonjhe. Iye watumidwa ni atumiki a kumwamba a Mnungu kuti upite kukhomo kwake, kuti wavechele mau yayo siumkambile.” 23Petulo wadaakambila wandhu wajha kuti akhale mnyumba mujha usiku wonjhe.
Siku lakawili wadapita pamojhi ni anyiiwo ni wandhu wina adamkhulupilila Kilisito ku Yopa.
24Siku la kawili wadafika ku Kaisaliya, uko Konelio wamamlindila, pamojhi ni abale ni abwenji apafupi yao wadaalalika. 25Petulo yapo wadawandikila kulowa mkati, Konelio wadachoka kuti wamulandile, wadamugwela Petulo mmyendo ni kumlambila. 26Nambho Petulo wadamuimika ni kumkambila, “Ima, ine chinchijha ni mundhupe ngati iwe.” 27Petulo wadayendekela kukamba ni Konelio yapo wamalowa mkati, umo wadaaona wandhu ambili asonghana. 28Petulo wadaakambila, “Mjhiwa bwino khalidwe la Ayahudi kuti siifunika kugwilizana ni wandhu osati Ayahudi kapina kwaayendela. Nambho Mnungu wanilangiza kuti sinidamtana mundhu waliyonjhe kuti osavomelezeka kumlambila Mnungu kapina wosati woyela. 29Chimwecho yapo mdanitana sinidakane kujha. Chipano nikufunjhani, mwanitanila chiyani?”
30Konelio wadayangha, “Masiku yatatu yayo yapita, nidali pakhomo kupembhela ndhawi ngati ino ya saa tisa. Mwachizulumukila nidaona mundhu wavala njhalu zong'azikila mbuu waima pachogolo panga, 31ni kukamba, ‘Konelio, Mnungu wavela mapembhelo yako ni njhembe zako izo wapacha wosauka Mnungu wazikumbukila. 32Atume wandhu apite ku Yopa, akamtane Simoni uyo watanidwa Petulo. Iye ni mlendo pa nyumba ya Simoni wokonja vikwetu, uyo wakhala pafupi ni nyanja ya mchele.’ 33Chimwecho nidaatuma wandhu chisanga kujha kwako, nawe wachita bwino kujha. Chipano iwe taonjhe tili pano pamaso pa Mnungu, tilindila kuvela kandhu kalikonjhe yako akutuma Amnungu ukambe.”
Petulo wauzila
34Pamenepo Petulo wadayamba kufotokoza, “Zene nijhiwa kuti Mnungu siwasangha. 35Nambho mundhu wa jhiko lalilonjhe uyo wamalambila Mnungu ni kuchita vovomelezeka walandilidwa ni iye. 36Anyiimwe muujhiwa uthenga uwo wadaupeleka Mnungu wa wandhu a ku Izilaeli, niwauzila uthenga wabwino uwo upeleka mtendele kupitila Yesu Kilisito, uyo wali Ambuye wa onjhe. 37Anyiimwe Mujhiwa vonjhe ivo vidachitika mu jhiko lonjhe la Ayahudi kuyambila ku Galilaya uko Yohana wadalalikila nghani ya ubatizi. 38Mujhiwa nghani za Yesu wa ku Nazaleti ni umo Mnungu wadampacha Mzimu Woyela ni ulamuli. Pakuti Mnungu wadali pamojhi ni iye kila kumalo uko wadapita, niwachita vabwino ni kulamicha wandhu wonjhe yawo adali panjhi pa mbhavu za Satana. 39Ife ni amboni a vindhu vonjhe ivo wadavichita mu Yudea ni mu Yelusalemu. Ndiipo achogoleli adampha ni kumpachika pa mtanda. 40Nambho Mnungu wadamhyukicha siku la katatu ni kumchita waoneke kwa wandhu, 41siwadaonekane kwa wandhu wonjhe, nambho kwa ife amboni okha yawo Mnungu wadathotisangha ife tidamwa ni kumwa pamojhi ni iye yapo wadahyuka. 42Nayo wadatiagiza tilalikile wandhu uthenga wa Bwino ni kuchochocha umboni kuti Yesu nde uyo wamsanghidwa kukhala mlamuli wa amoyo ni akufa. 43Alosi wonjhe adakamba nghani zake, niakamba waliyonjhe uyo siwamkhulupilile Yesu siwalekeleledwe machimo yake kwa njila yake.”
Konelio ni achaabale wake amlandila Mzimu Woyela
44Petulo yapo wadali wakali kukamba chimwecho, Mzimu Woyela udaachikila wandhu wonjhe yawo amavechela uthenga wake. 45Ayahudi yawo adakhulupilila ni kujha ni Petulo kuchokela ku Yopa adazizwa kuona Mnungu wachicha mbhaso yake ya Mzimu Woyela mbaka kwa wandhu osati Ayahudi. 46Adajhiwa chimwecho ndande wadaavela niakamba mikambo yachilendo ni kuutamanda ukulu wa Mnungu. Ndiipo Petulo wadakamba, 47“Wandhu anyiyawa alandila Mzimu Woyela, ngati umo tidamlandilila ife. Bwanji, pali mundhu waliyonjhe uyo wakhoza kukaniza kuti saadabatizidwa kwa majhi?” 48Chimwecho wadalamula kuti abatizidwe kwa jhina la Yesu Kilisito. Basi wandhu anyiwajha adampembha Petulo wakhale ni anyiiwo kwa masiku yochepa.
ទើបបានជ្រើសរើសហើយ៖
Vichito 10: NTNYBL2025
គំនូសចំណាំ
ចែករំលែក
ចម្លង
ចង់ឱ្យគំនូសពណ៌ដែលបានរក្សាទុករបស់អ្នក មាននៅលើគ្រប់ឧបករណ៍ទាំងអស់មែនទេ? ចុះឈ្មោះប្រើ ឬចុះឈ្មោះចូល
The New Testament in Nyanja @The Word for The World International and Nyanja Language translation, 2025. All rights reserved.